NSANJA YA OLONDA May 2013 | Kodi Mulungu ndi Wankhanza?

Masoka achilengedwe omwe amachitika masiku ano komanso zilango zimene Mulungu ankapereka zimene zinalembedwa m’Baibulo zimachititsa anthu kuganiza kuti Mulungu ndi wankhanza. Kodi umboni umasonyeza kuti Mulungu ndi wankhanza?

NKHANI YAPACHIKUTO

N’chifukwa Chiyani Ena Amati Mulungu Ndi Wankhanza?

Anthu ambiri amaona kuti Mulungu ndi wankhanza kapena alibe chidwi ndi anthu. Kodi Baibulo limati chiyani pa nkhaniyi?

NKHANI YAPACHIKUTO

Masoka Achilengedwe Kodi Ndi Umboni Wakuti Mulungu Ndi Wankhanza?

Ngatidi Mulungu amadana ndi zoipa, n’chifukwa chiyani amalola kuti anthu osalakwa azifa chifukwa cha masoka achilengedwe?

NKHANI YAPACHIKUTO

Zilango za Mulungu Kodi Zimasonyeza Kuti Ndi Wankhanza?

Kuti tiyankhe funso limeneli, tiganizire kaye zitsanzo ziwiri zotchulidwa m’Baibulo zomwe ndi Chigumula cha Nawa komanso kuwonongedwa kwa anthu a ku Kanani.

NKHANI YAPACHIKUTO

Muzikhulupirira Mulungu

Werengani kuti mudziwe mmene mungapindulire chifukwa chodziwa Mulungu ngati mnzanu wapamtima.

BAIBULO LIMASINTHA ANTHU

”Ndinkafuna Kudzakhala Wansembe”

Kuyambira ali mwana, Roberto Pacheco ankafunitsitsa kudzakhala wansembe wa Katolika. Werengani kuti mudziwe zomwe zinachititsa kuti zinthu zisinthe pa moyo wake.

CHINSINSI CHA BANJA LOSANGALALA

Zimene Banja la Ana Opeza Lingachite Kuti Lizigwirizana ndi Anthu Ena

Kodi mfundo za m’Baibulo zingathandize bwanji makolo a m’banja la ana opeza kuti azigwirizana ndi anzawo, achibale komanso makolo enieni a anawo?

YANDIKIRANI MULUNGU

Kodi Yehova Amakuganizirani?

Kodi zimakuvutani kukhulupirira kuti Mulungu amakuonani kuti ndinu wofunika kwambiri? Mawu a Yesu pa Yohane 6:44 amasonyeza kuti Mulungu amakuganizirani kwambiri inuyo panokha.

Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Kodi Mulungu amakhululukira ngakhale machimo aakulu? Kodi tiyenera kuchita chiyani kuti Mulungu azitikonda?

Choonadi

Kodi tingachipeze kuti? Kodi chingakuthandizeni bwanji komanso banja lanu? Tikukuitanani kuti mudzamve mayankho a mafunso amenewa pa msonkhano umene udzachitike masiku atatu.

Zina zimene zili pawebusaiti

Kodi a Mboni za Yehova Amakhulupirira Kuti Ndiwo Okha Amene Adzapulumuke?

Baibulo limafotokoza za anthu amene angakhale ndi mwayi wodzapulumuka