Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Ntchito Zanu N’zodabwitsa

Ntchito Zanu N’zodabwitsa

Pangani Dawunilodi:

  1. 1. Ntchito za ufumu zadziwikadi konse,

    Mwaphunzitsa cho’nadi kuyambira m’mbuyo monse.

    Kapolo wanu wanzeru, amawunikira

    Amandipatsa ‘busawa ondilimbikitsa.

    Zomwe timadikira zimachitikadi.

    Msonkhanotu uliwonse, umaposa yonse!

    Mlungu uliwonse timaphunzira za inu

    Ndiponso kulalikira anthu kulikonse.

    (KOLASI)

    Ntchito zanu zonse

    N’zodabwitsadi Yehova.

    Ufumu wayamba,

    Ndipo timazindikira ndinudi Mulungu.

    Tikudikira Madalitso a ufumuwu.

  2. 2. Mwatilemekeza pogwira nanu ntchito.

    Ndi utumikiwu timasonyeza chikondi.

    Mwatipatsa mtendere, tadziwanso zozama

    Zimathandiza kukhala anthu abwinodi.

    Ndikamvera nyimbo zathu ndimamva bwino

    Kulambira kwa pabanjanso n’kothandizadi.

    Ubale wathu padziko lonse ukutheka,

    Izi n’zochititsa chidwi, n’zosowa m’dzikoli.

    (KOLASI)

    Ntchito zanu zonse

    N’zodabwitsadi Yehova.

    Ufumu wayamba,

    Ndipo timazindikira ndinudi Mulungu.

    Tikudikira Madalitso a ufumuwu.