Tizikhululukilana
Daunilodi:
1. Munali kufuna zabwino
Mumanicitilanso cifundo
Koma munasokoneza mawu
Moti misozi ikugwa
Sitinamvetsetsane
(KOLASI)
Dzuŵali lisanangene
Nabwela tikambitsilane
Tikhululukilane tisazondane
Tikhalebe mwamtendele
2. Kugwilizana nikovutadi
Mawu olatsa mtima aŵaŵa
Koma kukhululukilana
Ndiye kungatithandize
Kukhala na mtendele
(KOLASI)
Dzuŵali lisanangene
Nabwela tikambitsilane
Tikhululukilane tisazondane
Tikhalebe mwamtendele
(BILIJI)
Palibe cimene cingalekanitse
Ubale wathu
Iŵalako, khululukadi
Tizalimbitsa ubwenzi
(KOLASI)
Dzuŵali lisanangene
Nabwela tikambitsilane
Tikhululukilane tisazondane
Tikhalebe mwamtendele
Mwacikondi, tikhululukilane